Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 41:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Wodala iye amene asamalira wosauka:Tsiku la tsoka Yehova adzampulumutsa:

2. Yehova adzamsunga, nadzamsunga ndi moyo, ndipo adzadalitsika pa dziko lapansi;Ndipo musampereke ku cifuniro ca adani ace.

3. Yehova adzamgwiriziza pa kama wodwalira;Podwala iye mukonza pogona pace,

4. Ndinati ine, Mundicitire cifundo, Yehova:Ciritsani mtima wanga; pakuti ndacimwira Inu.

5. Adani anga andinenera coipa, ndi kuti,Adzafa liti, ndi kutayika dzina lace?

6. Ndipo akadza kundiona wina angonena bodza;Mumtima mwace adzisonkhera zopanda pace:Akamka nayenda namakanena:

7. Onse akudana nane andinong'onezerana;Apangana condiipsa ine.

8. Camgwera cinthu coopsa, ati;Popeza ali gonire sadzaukanso.

9. Ngakhale bwenzi langa leni leni, amene ndamkhulupirira, ndiye amene adadyako mkate wanga,Anandikwezera cidendene cace.

10. Koma Inu, Yehova, mundicitire cifundo, ndipo mundiutse,Kuti ndiwabwezere.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 41