Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 39:3-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Mtima wanga unatentha m'kati mwaine;Unayaka moto pakulingirira ine:Pamenepo ndinalankhula ndi lilime langa:

4. Yehova, mundidziwitse cimariziro canga,Ndi mawerengedwe a masiku anga ndi angati;Ndidziwe malekezero anga,

5. Onani, munaika masiku anga akhale monga kuyesa dzanja;Ndipo zaka zanga ziri ngati cabe pamaso panu:Indedi munthu ali yense angakhale wokhazikika, ali cabe konse.

6. Indedi munthu ayenda ngati mthunzi:Indedi abvutika cabe:Asonkhanitsa cuma, ndipo sadziwa adzacilandira ndani?

7. Ndipo tsopano, Ambuye, ndilindira ciani?Ciyembekezo canga ciri pa Inu.

8. Ndipulumutseni kwa zolakwa zangazonse:Musandiike ndikhale cotonza ca wopusa.

9. Ndinakhala du, sindinatsegula pakamwa panga;Cifukwa inu mudacicita.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 39