Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 38:5-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Mabala anga anunkha, adaola, Cifukwa ca kupusa kwanga.

6. Ndapindika, ndawerama kwakukuru;Ndimayenda woliralira tsiku lonse.

7. Pakuti m'cuuno mwanga mutentha kwambiri;Palibe pamoyo m'mnofu mwanga,

8. Ndafoka ine, ndipo ndacinjizidwa:Ndabangula cifukwa ca kumyuka mtima wanga.

9. Ambuye, cikhumbo canga conse ciri pamaso panu;Ndipo kubuula kwanga sikubisika kwa Inu.

10. Mtima wanga ugundagunda, mphamvu yanga yacoka:Ndipo kuunika kwa maso anga, ndi iko komwe kwandicokera.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 38