10. Mtima wanga ugundagunda, mphamvu yanga yacoka:Ndipo kuunika kwa maso anga, ndi iko komwe kwandicokera.
11. Ondikonda ndi anzanga apewa mliri wanga;Ndipo anansi anga aima patali.
12. Ndipo andichera misampha iwo akufuna moyo wanga;Ndipo iwo akuyesa kundicitira coipa alankhula zoononga,Nalingirira zonyenga tsiku lonse.
13. Koma ine, monga gonthi, sindimva;Ndipo monga munthu wosalankhula, sinditsegula pakamwa panga.
14. Inde ndikunga munthu wosamva,Ndipo m'kamwa mwanga mulibe makani.
15. Pakuti ndikuyembekezani Inu, Yehova;Inu mudzayankha, Ambuye Mulungu wanga.
16. Pakuti ndinati, Asakondwerere ine:Pakuterereka phazi langa, asadzikuze pa ine.