1. Yehova, musandidzudzule ndi mkwiyo wanu:Ndipo musandilange moopsa m'mtima mwanu.
2. Pakuti mibvi yanu yandilowa,Ndi dzanja lanu landigwera.
3. Mumnofu mwanga mulibe camoyo cifukwa ca ukali wanu;Ndipo m'mafupa anga simuzizira, cifukwa ca colakwa canga.
4. Pakuti mphulupulu zanga zapitirira pamutu panga:Ndathodwa nazo monga ndi katundu wolemera.
5. Mabala anga anunkha, adaola, Cifukwa ca kupusa kwanga.
6. Ndapindika, ndawerama kwakukuru;Ndimayenda woliralira tsiku lonse.
7. Pakuti m'cuuno mwanga mutentha kwambiri;Palibe pamoyo m'mnofu mwanga,
8. Ndafoka ine, ndipo ndacinjizidwa:Ndabangula cifukwa ca kumyuka mtima wanga.
9. Ambuye, cikhumbo canga conse ciri pamaso panu;Ndipo kubuula kwanga sikubisika kwa Inu.
10. Mtima wanga ugundagunda, mphamvu yanga yacoka:Ndipo kuunika kwa maso anga, ndi iko komwe kwandicokera.
11. Ondikonda ndi anzanga apewa mliri wanga;Ndipo anansi anga aima patali.
12. Ndipo andichera misampha iwo akufuna moyo wanga;Ndipo iwo akuyesa kundicitira coipa alankhula zoononga,Nalingirira zonyenga tsiku lonse.
13. Koma ine, monga gonthi, sindimva;Ndipo monga munthu wosalankhula, sinditsegula pakamwa panga.
14. Inde ndikunga munthu wosamva,Ndipo m'kamwa mwanga mulibe makani.
15. Pakuti ndikuyembekezani Inu, Yehova;Inu mudzayankha, Ambuye Mulungu wanga.