Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 37:9-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Pakuti ocita zoipa adzadulidwa:Koma iwo akuyembekeza Yehova, iwowa adzalandira dziko lapansi.

10. Katsala kanthawi ndipo woipa adzatha psiti:Inde, udzayang'anira mbuto yace, nudzapeza palibe.

11. Koma ofatsa adzalandira dziko lapansi;Nadzakondwera nao mtendere wocuruka.

12. Woipa apangira ciwembu wolungama,Namkukutira mano.

13. Ambuye adzamseka:Popeza apenya kuti tsiku lace likudza.

14. Oipa anasolola lupanga, nakoka uta wao;Alikhe ozunzika ndi aumphawi,Aphe amene ali oongoka m'njira:

15. Lupanga lao lidzalowa m'mtima mwao momwe,Ndipo mauta ao adzatyoledwa.

16. Zocepa zace za wolungama zikomaKoposa kucuruka kwao kwa oipa ambiri.

17. Pakuti manja a oipa adzatyoledwa:Koma Yehova acirikiza olungama.

18. Yehova adziwa masiku a anthu angwiro:Ndipo cosiyira cao cidzakhala cosatha.

19. Sadzacita manyazi m'nyengo yoipa:Ndipo m'masiku a njala adzakhuta.

20. Pakuti oipa adzatayika,Ndipo adani ace a Yehova adzanga mafuta a ana a nkhosa:Adzanyeka, monga utsi adzakanganuka.

21. Woipa akongola, wosabweza:Koma wolungama acitira cifundo, napereka.

22. Pakuti iwo amene awadalitsa adzalandira dziko lapansi;Koma iwo amene awatemberera adzadulidwa.

23. Yehova akhazikitsa mayendedwe a munthu;Ndipo akondwera nayo njira yace.

24. Angakhale akagwa, satayikiratu:Pakuti Yehova agwira dzanja lace.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 37