8. Leka kupsa mtima, nutaye mkwiyo:Usabvutike mtima ungacite coipa,
9. Pakuti ocita zoipa adzadulidwa:Koma iwo akuyembekeza Yehova, iwowa adzalandira dziko lapansi.
10. Katsala kanthawi ndipo woipa adzatha psiti:Inde, udzayang'anira mbuto yace, nudzapeza palibe.
11. Koma ofatsa adzalandira dziko lapansi;Nadzakondwera nao mtendere wocuruka.
12. Woipa apangira ciwembu wolungama,Namkukutira mano.
13. Ambuye adzamseka:Popeza apenya kuti tsiku lace likudza.
14. Oipa anasolola lupanga, nakoka uta wao;Alikhe ozunzika ndi aumphawi,Aphe amene ali oongoka m'njira:
15. Lupanga lao lidzalowa m'mtima mwao momwe,Ndipo mauta ao adzatyoledwa.