34. Yembekeza Yehova, nusunge njira yace,Ndipo Iye adzakukweza kuti ulandire dziko:Pakudutidwa oipa udzapenya,
35. Ndapenya woipa, alikuopsa,Natasa monga mtengo wauwisi wanzika.
36. Koma anapita ndipo taona, kwati zi:Ndipo ndinampwaira osampeza.
37. Tapenya wangwiro, ndipo taona woongoka mtima!Pakuti ku matsiriziro ace a munthuyo kuti mtendere.
38. Koma olakwa adzaonongeka pamodzi:Matsiriziro a oipa adzadutidwa.
39. Koma cipulumutso ca olungama cidzera kwa Yehova,Iye ndiye mphamvu yao m'nyengo ya nsautso.
40. Ndipo Yehova awathandiza, nawalanditsa:Awalanditsa kwa oipa nawapulumutsa,Cifukwa kuti anamkhulupirira Iye,