Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 37:29-39 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Olungama adzalandira dziko lapansi,Nadzakhala momwemo kosatha.

30. Pakamwa pa wolungama palankhula zanzeru,Ndi lilime lace linena ciweruzo.

31. Malamulo a Mulungu wace ali mumtima mwace;Pakuyenda pace sadzaterereka.

32. Woipa aunguza wolungama,Nafuna kumupha.

33. Yehova sadzamsiya m'dzanja lace:Ndipo sadzamtsutsa poweruzidwa iye.

34. Yembekeza Yehova, nusunge njira yace,Ndipo Iye adzakukweza kuti ulandire dziko:Pakudutidwa oipa udzapenya,

35. Ndapenya woipa, alikuopsa,Natasa monga mtengo wauwisi wanzika.

36. Koma anapita ndipo taona, kwati zi:Ndipo ndinampwaira osampeza.

37. Tapenya wangwiro, ndipo taona woongoka mtima!Pakuti ku matsiriziro ace a munthuyo kuti mtendere.

38. Koma olakwa adzaonongeka pamodzi:Matsiriziro a oipa adzadutidwa.

39. Koma cipulumutso ca olungama cidzera kwa Yehova,Iye ndiye mphamvu yao m'nyengo ya nsautso.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 37