Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 37:28-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

28. Pakuti Yehova akonda ciweruzo,Ndipo sataya okondedwa ace:Asungika kosatha:Koma adzadula mbumba za oipa.

29. Olungama adzalandira dziko lapansi,Nadzakhala momwemo kosatha.

30. Pakamwa pa wolungama palankhula zanzeru,Ndi lilime lace linena ciweruzo.

31. Malamulo a Mulungu wace ali mumtima mwace;Pakuyenda pace sadzaterereka.

32. Woipa aunguza wolungama,Nafuna kumupha.

33. Yehova sadzamsiya m'dzanja lace:Ndipo sadzamtsutsa poweruzidwa iye.

34. Yembekeza Yehova, nusunge njira yace,Ndipo Iye adzakukweza kuti ulandire dziko:Pakudutidwa oipa udzapenya,

35. Ndapenya woipa, alikuopsa,Natasa monga mtengo wauwisi wanzika.

36. Koma anapita ndipo taona, kwati zi:Ndipo ndinampwaira osampeza.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 37