28. Pakuti Yehova akonda ciweruzo,Ndipo sataya okondedwa ace:Asungika kosatha:Koma adzadula mbumba za oipa.
29. Olungama adzalandira dziko lapansi,Nadzakhala momwemo kosatha.
30. Pakamwa pa wolungama palankhula zanzeru,Ndi lilime lace linena ciweruzo.
31. Malamulo a Mulungu wace ali mumtima mwace;Pakuyenda pace sadzaterereka.
32. Woipa aunguza wolungama,Nafuna kumupha.
33. Yehova sadzamsiya m'dzanja lace:Ndipo sadzamtsutsa poweruzidwa iye.