21. Woipa akongola, wosabweza:Koma wolungama acitira cifundo, napereka.
22. Pakuti iwo amene awadalitsa adzalandira dziko lapansi;Koma iwo amene awatemberera adzadulidwa.
23. Yehova akhazikitsa mayendedwe a munthu;Ndipo akondwera nayo njira yace.
24. Angakhale akagwa, satayikiratu:Pakuti Yehova agwira dzanja lace.
25. Ndinali mwana ndipo ndakalamba:Ndipo sindinapenya wolungama wasiyidwa,Kapena mbumba zace zirinkupempha cakudya.
26. Tsiku lonse acitira cifundo, nakongoletsa;Ndipo mbumba zace zidalitsidwa.
27. Siyana naco coipa, nucite cokoma,Nukhale nthawi zonse.
28. Pakuti Yehova akonda ciweruzo,Ndipo sataya okondedwa ace:Asungika kosatha:Koma adzadula mbumba za oipa.
29. Olungama adzalandira dziko lapansi,Nadzakhala momwemo kosatha.