20. Pakuti oipa adzatayika,Ndipo adani ace a Yehova adzanga mafuta a ana a nkhosa:Adzanyeka, monga utsi adzakanganuka.
21. Woipa akongola, wosabweza:Koma wolungama acitira cifundo, napereka.
22. Pakuti iwo amene awadalitsa adzalandira dziko lapansi;Koma iwo amene awatemberera adzadulidwa.
23. Yehova akhazikitsa mayendedwe a munthu;Ndipo akondwera nayo njira yace.
24. Angakhale akagwa, satayikiratu:Pakuti Yehova agwira dzanja lace.
25. Ndinali mwana ndipo ndakalamba:Ndipo sindinapenya wolungama wasiyidwa,Kapena mbumba zace zirinkupempha cakudya.
26. Tsiku lonse acitira cifundo, nakongoletsa;Ndipo mbumba zace zidalitsidwa.
27. Siyana naco coipa, nucite cokoma,Nukhale nthawi zonse.
28. Pakuti Yehova akonda ciweruzo,Ndipo sataya okondedwa ace:Asungika kosatha:Koma adzadula mbumba za oipa.
29. Olungama adzalandira dziko lapansi,Nadzakhala momwemo kosatha.
30. Pakamwa pa wolungama palankhula zanzeru,Ndi lilime lace linena ciweruzo.
31. Malamulo a Mulungu wace ali mumtima mwace;Pakuyenda pace sadzaterereka.
32. Woipa aunguza wolungama,Nafuna kumupha.
33. Yehova sadzamsiya m'dzanja lace:Ndipo sadzamtsutsa poweruzidwa iye.
34. Yembekeza Yehova, nusunge njira yace,Ndipo Iye adzakukweza kuti ulandire dziko:Pakudutidwa oipa udzapenya,
35. Ndapenya woipa, alikuopsa,Natasa monga mtengo wauwisi wanzika.