Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 37:2-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Pakuti adzawamweta msanga monga udzu,Ndipo adzafota monga msipu wauwisi.

3. Khulupirira Yehova, ndipo cita cokoma;Khala m'dziko, ndipo tsata coonadi.

4. Udzikondweretsenso mwa Yehova;Ndipo iye adzakupatsa zokhumba mtima wako.

5. Pereka njira yako kwa Yehova; Khulupiriranso Iye, adzacicita.

6. Ndipo adzaonetsa cilungamo cako monga kuunika,Ndi kuweruza kwako monga usana.

7. Khala cete mwa Yehova, numlindirire Iye:Usabvutike mtima cifukwa ca iye wolemerera m'njira yace,Cifukwa ca munthu wakucita ciwembu.

8. Leka kupsa mtima, nutaye mkwiyo:Usabvutike mtima ungacite coipa,

9. Pakuti ocita zoipa adzadulidwa:Koma iwo akuyembekeza Yehova, iwowa adzalandira dziko lapansi.

10. Katsala kanthawi ndipo woipa adzatha psiti:Inde, udzayang'anira mbuto yace, nudzapeza palibe.

11. Koma ofatsa adzalandira dziko lapansi;Nadzakondwera nao mtendere wocuruka.

12. Woipa apangira ciwembu wolungama,Namkukutira mano.

13. Ambuye adzamseka:Popeza apenya kuti tsiku lace likudza.

14. Oipa anasolola lupanga, nakoka uta wao;Alikhe ozunzika ndi aumphawi,Aphe amene ali oongoka m'njira:

15. Lupanga lao lidzalowa m'mtima mwao momwe,Ndipo mauta ao adzatyoledwa.

16. Zocepa zace za wolungama zikomaKoposa kucuruka kwao kwa oipa ambiri.

17. Pakuti manja a oipa adzatyoledwa:Koma Yehova acirikiza olungama.

18. Yehova adziwa masiku a anthu angwiro:Ndipo cosiyira cao cidzakhala cosatha.

19. Sadzacita manyazi m'nyengo yoipa:Ndipo m'masiku a njala adzakhuta.

20. Pakuti oipa adzatayika,Ndipo adani ace a Yehova adzanga mafuta a ana a nkhosa:Adzanyeka, monga utsi adzakanganuka.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 37