Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 37:2-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Pakuti adzawamweta msanga monga udzu,Ndipo adzafota monga msipu wauwisi.

3. Khulupirira Yehova, ndipo cita cokoma;Khala m'dziko, ndipo tsata coonadi.

4. Udzikondweretsenso mwa Yehova;Ndipo iye adzakupatsa zokhumba mtima wako.

5. Pereka njira yako kwa Yehova; Khulupiriranso Iye, adzacicita.

6. Ndipo adzaonetsa cilungamo cako monga kuunika,Ndi kuweruza kwako monga usana.

7. Khala cete mwa Yehova, numlindirire Iye:Usabvutike mtima cifukwa ca iye wolemerera m'njira yace,Cifukwa ca munthu wakucita ciwembu.

8. Leka kupsa mtima, nutaye mkwiyo:Usabvutike mtima ungacite coipa,

9. Pakuti ocita zoipa adzadulidwa:Koma iwo akuyembekeza Yehova, iwowa adzalandira dziko lapansi.

10. Katsala kanthawi ndipo woipa adzatha psiti:Inde, udzayang'anira mbuto yace, nudzapeza palibe.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 37