Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 37:19-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Sadzacita manyazi m'nyengo yoipa:Ndipo m'masiku a njala adzakhuta.

20. Pakuti oipa adzatayika,Ndipo adani ace a Yehova adzanga mafuta a ana a nkhosa:Adzanyeka, monga utsi adzakanganuka.

21. Woipa akongola, wosabweza:Koma wolungama acitira cifundo, napereka.

22. Pakuti iwo amene awadalitsa adzalandira dziko lapansi;Koma iwo amene awatemberera adzadulidwa.

23. Yehova akhazikitsa mayendedwe a munthu;Ndipo akondwera nayo njira yace.

24. Angakhale akagwa, satayikiratu:Pakuti Yehova agwira dzanja lace.

25. Ndinali mwana ndipo ndakalamba:Ndipo sindinapenya wolungama wasiyidwa,Kapena mbumba zace zirinkupempha cakudya.

26. Tsiku lonse acitira cifundo, nakongoletsa;Ndipo mbumba zace zidalitsidwa.

27. Siyana naco coipa, nucite cokoma,Nukhale nthawi zonse.

28. Pakuti Yehova akonda ciweruzo,Ndipo sataya okondedwa ace:Asungika kosatha:Koma adzadula mbumba za oipa.

29. Olungama adzalandira dziko lapansi,Nadzakhala momwemo kosatha.

30. Pakamwa pa wolungama palankhula zanzeru,Ndi lilime lace linena ciweruzo.

31. Malamulo a Mulungu wace ali mumtima mwace;Pakuyenda pace sadzaterereka.

32. Woipa aunguza wolungama,Nafuna kumupha.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 37