Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 37:18-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Yehova adziwa masiku a anthu angwiro:Ndipo cosiyira cao cidzakhala cosatha.

19. Sadzacita manyazi m'nyengo yoipa:Ndipo m'masiku a njala adzakhuta.

20. Pakuti oipa adzatayika,Ndipo adani ace a Yehova adzanga mafuta a ana a nkhosa:Adzanyeka, monga utsi adzakanganuka.

21. Woipa akongola, wosabweza:Koma wolungama acitira cifundo, napereka.

22. Pakuti iwo amene awadalitsa adzalandira dziko lapansi;Koma iwo amene awatemberera adzadulidwa.

23. Yehova akhazikitsa mayendedwe a munthu;Ndipo akondwera nayo njira yace.

24. Angakhale akagwa, satayikiratu:Pakuti Yehova agwira dzanja lace.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 37