18. Yehova adziwa masiku a anthu angwiro:Ndipo cosiyira cao cidzakhala cosatha.
19. Sadzacita manyazi m'nyengo yoipa:Ndipo m'masiku a njala adzakhuta.
20. Pakuti oipa adzatayika,Ndipo adani ace a Yehova adzanga mafuta a ana a nkhosa:Adzanyeka, monga utsi adzakanganuka.
21. Woipa akongola, wosabweza:Koma wolungama acitira cifundo, napereka.
22. Pakuti iwo amene awadalitsa adzalandira dziko lapansi;Koma iwo amene awatemberera adzadulidwa.
23. Yehova akhazikitsa mayendedwe a munthu;Ndipo akondwera nayo njira yace.
24. Angakhale akagwa, satayikiratu:Pakuti Yehova agwira dzanja lace.