12. Woipa apangira ciwembu wolungama,Namkukutira mano.
13. Ambuye adzamseka:Popeza apenya kuti tsiku lace likudza.
14. Oipa anasolola lupanga, nakoka uta wao;Alikhe ozunzika ndi aumphawi,Aphe amene ali oongoka m'njira:
15. Lupanga lao lidzalowa m'mtima mwao momwe,Ndipo mauta ao adzatyoledwa.
16. Zocepa zace za wolungama zikomaKoposa kucuruka kwao kwa oipa ambiri.
17. Pakuti manja a oipa adzatyoledwa:Koma Yehova acirikiza olungama.
18. Yehova adziwa masiku a anthu angwiro:Ndipo cosiyira cao cidzakhala cosatha.