Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 37:1-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Usabvutike mtima cifukwa ca ocita zoipa,Usacite nsanje cifukwa ca ocita cosalungama.

2. Pakuti adzawamweta msanga monga udzu,Ndipo adzafota monga msipu wauwisi.

3. Khulupirira Yehova, ndipo cita cokoma;Khala m'dziko, ndipo tsata coonadi.

4. Udzikondweretsenso mwa Yehova;Ndipo iye adzakupatsa zokhumba mtima wako.

5. Pereka njira yako kwa Yehova; Khulupiriranso Iye, adzacicita.

6. Ndipo adzaonetsa cilungamo cako monga kuunika,Ndi kuweruza kwako monga usana.

7. Khala cete mwa Yehova, numlindirire Iye:Usabvutike mtima cifukwa ca iye wolemerera m'njira yace,Cifukwa ca munthu wakucita ciwembu.

8. Leka kupsa mtima, nutaye mkwiyo:Usabvutike mtima ungacite coipa,

9. Pakuti ocita zoipa adzadulidwa:Koma iwo akuyembekeza Yehova, iwowa adzalandira dziko lapansi.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 37