1. Usabvutike mtima cifukwa ca ocita zoipa,Usacite nsanje cifukwa ca ocita cosalungama.
2. Pakuti adzawamweta msanga monga udzu,Ndipo adzafota monga msipu wauwisi.
3. Khulupirira Yehova, ndipo cita cokoma;Khala m'dziko, ndipo tsata coonadi.
4. Udzikondweretsenso mwa Yehova;Ndipo iye adzakupatsa zokhumba mtima wako.
5. Pereka njira yako kwa Yehova; Khulupiriranso Iye, adzacicita.
6. Ndipo adzaonetsa cilungamo cako monga kuunika,Ndi kuweruza kwako monga usana.