Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 35:1-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Tsutsanani nao iwo akutsutsana nane, Yehova:Limbanani nao iwo akulimbana nane.

2. Gwirani cikopa cocinjiriza, Ukani kundithandiza.

3. Sololani nthungo, ndipo muwatsekerezere kunjira akundilondola:Nenani ndi moyo wanga, Cipulumutso cako ndine.

4. Athe nzeru nacite manyazi iwo akufuna moyo wanga:Abwezedwe m'mbuyo nasokonezeke iwo akundipangira ciwembu.

5. Akhale monga mungu kumphepo,Ndipo mngelo wa Yehova awapitikitse.

6. Njira yao ikhale ya mdima ndi yoterera,Ndipo mngelo wa Yehova awalondole.

7. Pakuti anandichera ukonde wao m'mbunamo kopanda cifukwa,Anakumbira moyo wanga dzenje kopanda cifukwa.

8. Cimgwere modzidzimutsa cionongeko;Ndipo ukonde wace umene anaucha umkole yekha mwini:Agwemo, naonongeke m'mwemo.

9. Ndipo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova:Udzasekera mwa cipulumutso cace.

10. Mafupa anga onse adzanena, Yehova, afanana ndi Inu ndani,Wakulanditsa wozunzika kwa iye amene amposa mphamvu,Ndi wozunzika ndi waumphawi kwa iye amfunkhira?

11. Mboni za ciwawa ziuka,Zindifunsa zosadziwa ine.

12. Andibwezera coipa m'malo mwa cokoma,Inde, asaukitsa moyo wanga.

13. Koma ine, pakudwala iwowa, cobvala canga ndi ciguduli:Ndinazunza moyo wanga ndi kusala;Ndipo pemphero langa linabwera ku cifuwa canga.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 35