Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 34:8-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Talawani, ndipo onani kuti Yehova ndiye wabwino;Wodala munthuyo wakukhulupirira Iye.

9. Opani Yehova, inu oyera mtima ace;Cifukwa iwo akumuopa Iye sasowa.

10. Misona ya mkango isowa nimva njala:Koma iwo akufuna Yehova sadzasowa kanthu kabwino.

11. Idzani ananu ndimvereni ine:Ndidzakulangizani zakumuopa Yehova.

12. Munthu wokhumba moyo ndani,Wokonda masiku, kuti aone zabwino?

13. Uletse lilime lako lisachule zoipa,Ndipo milomo yako isalankhule cinyengo.

14. Pfutuka pazoipa, nucite zabwino,Funa mtendere ndi kuulondola.

15. Maso a Yehova ali pa olungama mtima,Ndipo makutu ace achereza kulira kwao.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 34