Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 34:5-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Iwo anayang'ana Iye nasanguruka;Ndipo pankhope pao sipadzacita manyazi,

6. Munthu uyu wozunzika anapfuula, ndipo Yehova anamumva,Nampulumutsa m'masautso ace onse.

7. Mngelo wa Yehova azinga kuwacinjiriza iwo akuopa Iye,Nawalanditsa iwo.

8. Talawani, ndipo onani kuti Yehova ndiye wabwino;Wodala munthuyo wakukhulupirira Iye.

9. Opani Yehova, inu oyera mtima ace;Cifukwa iwo akumuopa Iye sasowa.

10. Misona ya mkango isowa nimva njala:Koma iwo akufuna Yehova sadzasowa kanthu kabwino.

11. Idzani ananu ndimvereni ine:Ndidzakulangizani zakumuopa Yehova.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 34