Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 32:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Wodala munthuyo wokhululukidwa chimo lace;Wokwiriridwa coipa cace.

2. Wodala munthuyu Yehova samwerengera mphulupulu zace;Ndimo mumzimu mwace mulibe cinyengo.

3. Pamene ndinakhala cete mafupa anga anakalambaNdi kubuula kwanga tsiku lonse.

4. Cifukwa usana ndi usiku dzanja lanu linandilemera ine;Uwisi wanga unasandulika kuuma kwa malimwe.

5. Ndinabvomera coipa canga kwa Inu;Ndipo mphulupulu yanga sindinaibisa.Ndinati, Ndidzaululira Yehova macimo anga;Ndipo munakhululukira coipa ca kulakwa kwanga.

6. Cifukwa cace oyera mtima onse apemphere kwa Inu,Pa nthawi ya kupeza Inu:Indetu pakusefuka madzi akuruSadzamfikira iye.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 32