Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 32:1-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Wodala munthuyo wokhululukidwa chimo lace;Wokwiriridwa coipa cace.

2. Wodala munthuyu Yehova samwerengera mphulupulu zace;Ndimo mumzimu mwace mulibe cinyengo.

3. Pamene ndinakhala cete mafupa anga anakalambaNdi kubuula kwanga tsiku lonse.

4. Cifukwa usana ndi usiku dzanja lanu linandilemera ine;Uwisi wanga unasandulika kuuma kwa malimwe.

5. Ndinabvomera coipa canga kwa Inu;Ndipo mphulupulu yanga sindinaibisa.Ndinati, Ndidzaululira Yehova macimo anga;Ndipo munakhululukira coipa ca kulakwa kwanga.

6. Cifukwa cace oyera mtima onse apemphere kwa Inu,Pa nthawi ya kupeza Inu:Indetu pakusefuka madzi akuruSadzamfikira iye.

7. Inu ndinu mobisalira mwanga; M'nsautso mudzandisunga;Mudzandizinga ndi Nyimbo za cipulumutso.

8. Ine ndidzakulangiza ndi kuphunzitsa iwe za njira ukayendayo;Ndidzakupangira ndi diso langa lakuyang'ana iwe.

9. Musakhale monga kavalo, kapena ngati buru, wopanda nzeru:Zomangira zao ndizo cam'kamwa ndi capamutu zakuwakokera,Pakuti ukapanda kutero sadzakuyandikiza.

10. Zisoni zambiri zigwera woipa:Koma cifundo cidzamzinga iye wakukhulupirira Yehova.

11. Sekerani mwa Yehova, ndimo kondwerani inu olungama mtima;Ndipo pfuulani mokondwera nonsenu oongoka mtima.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 32