1. Aphokoseranji amitundu.Nalingiriranji anthu zopanda pace?
2. Adzikhazikitsa mafumu a dziko lapansi,Nacita upo akulu pamodzi,Kutsutsana naye Yehova, ndi Wodzozedwa wace, ndi kuti.
3. Tidule zomangira zao,Titaye nsinga zao.
4. Wokhala m'mwambayo adzaseka;Ambuye adzawanyoza.
5. Pomwepo adzalankhula nao mu mkwiyo wace,Nadzawaopsa m'ukali wace:
6. Koma Ine ndadzoza mfumu yangaPa Ziyoni, phiri langa loyera.