Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 18:8-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Unakwera utsi woturuka m'mphuno mwace:Ndi moto wa m'kamwa mwace unanyeka:Nuyakitsa makara.

9. Ndipo Iye anaweramitsa thambo, natsika;Ndipo pansi pa mapazi ace panali mdima bii.

10. Ndipo anaberekeka pa kerubi, nauluka;Nauluka msanga pa mapiko a mphepo,

11. Anaika mdima pobisala pace, hema wace womzinga;Mdima wa madzi, makongwa a kuthambo.

12. Mwa kucezemira kunali pamaso pace makongwa anakanganuka,Matalala ndi makala amoto.

13. Ndipo anagunda m'mwamba Yehova,Ndipo Wam'mwambamwamba anamvetsa liu lace;Matalala ndi makala amoto,

14. Ndipo anatuma mibvi yace nawabalalitsa;Inde mphezi zaunyinji, nawamwaza.

15. Ndipo zidaoneka zoyendamo madzi,Nafukuka maziko a dziko lapansi,Mwa kudzudzula kwanu, Yehova,Mwa mpumo wa mpweya wa m'mphuno mwanu.

16. Anatuma kucokera m'mwamba, ananditenga;Anandibvuula m'madzi ambiri.

17. Anandipulumutsa ine kwa mdani wanga wamphamvu,Ndi kwa iwo ondida ine, pakuti anandiposa mphamvu.

18. Anandipeza ine tsiku la tsoka langa;Koma Yehova anali mcirikizo wanga.

19. Ananditurutsanso andifikitse motakasuka;Anandilanditsa, pakuti anakondwera ndi ine.

20. Yehova anandibwezera monga mwa cilungamo canga;Anandisudzula monga mwa kusisira kwa manja anga.

21. Pakuti ndasunga njira za Yehova,Ndipo sindinacitira coipa kusiyana ndi Mulungu wanga.

22. Pakuti maweruzo ace onse anali pamaso panga,Ndipo malemba ace sindinawacotsa kwa ine.

23. Ndipo ndinakhala wangwiro ndi iye,Ndipo ndinadzisunga wosacita coipa canga.

24. Ndimo anandisudzulira Yehova monga mwa cilungamo canga,Monga mwa kusisira kwa manja anga pamaso pace.

25. Pa wacifundo mukhala wacifundoPa mumthu wangwiro mukhala wangwiro;

Werengani mutu wathunthu Masalmo 18