4. Zingwe za imfa zinandizinga,Ndipo mitsinje ya zopanda pace inandiopsa.
5. Zingwe za manda zinandizinga:Misampha ya imfa inandifikira ine.
6. M'kusauka kwanga ndinaitana Yehova,Ndipo ndinakuwira Mulungu wanga;Mau anga anawamva m'Kacisi mwace,Ndipo mkuwo wanga wa pankhope pace unalowa m'makutu mwace.
7. Pamenepo linagwedezeka, ndi kutenthemera dziko lapansi.Ndi maziko a mapiri ananjenjemeraNagwedezeka, pakuti anakwiya iyeyo.
8. Unakwera utsi woturuka m'mphuno mwace:Ndi moto wa m'kamwa mwace unanyeka:Nuyakitsa makara.
9. Ndipo Iye anaweramitsa thambo, natsika;Ndipo pansi pa mapazi ace panali mdima bii.
10. Ndipo anaberekeka pa kerubi, nauluka;Nauluka msanga pa mapiko a mphepo,
11. Anaika mdima pobisala pace, hema wace womzinga;Mdima wa madzi, makongwa a kuthambo.
12. Mwa kucezemira kunali pamaso pace makongwa anakanganuka,Matalala ndi makala amoto.
13. Ndipo anagunda m'mwamba Yehova,Ndipo Wam'mwambamwamba anamvetsa liu lace;Matalala ndi makala amoto,
14. Ndipo anatuma mibvi yace nawabalalitsa;Inde mphezi zaunyinji, nawamwaza.
15. Ndipo zidaoneka zoyendamo madzi,Nafukuka maziko a dziko lapansi,Mwa kudzudzula kwanu, Yehova,Mwa mpumo wa mpweya wa m'mphuno mwanu.
16. Anatuma kucokera m'mwamba, ananditenga;Anandibvuula m'madzi ambiri.
17. Anandipulumutsa ine kwa mdani wanga wamphamvu,Ndi kwa iwo ondida ine, pakuti anandiposa mphamvu.