16. Anatuma kucokera m'mwamba, ananditenga;Anandibvuula m'madzi ambiri.
17. Anandipulumutsa ine kwa mdani wanga wamphamvu,Ndi kwa iwo ondida ine, pakuti anandiposa mphamvu.
18. Anandipeza ine tsiku la tsoka langa;Koma Yehova anali mcirikizo wanga.
19. Ananditurutsanso andifikitse motakasuka;Anandilanditsa, pakuti anakondwera ndi ine.
20. Yehova anandibwezera monga mwa cilungamo canga;Anandisudzula monga mwa kusisira kwa manja anga.
21. Pakuti ndasunga njira za Yehova,Ndipo sindinacitira coipa kusiyana ndi Mulungu wanga.