Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 18:14-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndipo anatuma mibvi yace nawabalalitsa;Inde mphezi zaunyinji, nawamwaza.

15. Ndipo zidaoneka zoyendamo madzi,Nafukuka maziko a dziko lapansi,Mwa kudzudzula kwanu, Yehova,Mwa mpumo wa mpweya wa m'mphuno mwanu.

16. Anatuma kucokera m'mwamba, ananditenga;Anandibvuula m'madzi ambiri.

17. Anandipulumutsa ine kwa mdani wanga wamphamvu,Ndi kwa iwo ondida ine, pakuti anandiposa mphamvu.

18. Anandipeza ine tsiku la tsoka langa;Koma Yehova anali mcirikizo wanga.

19. Ananditurutsanso andifikitse motakasuka;Anandilanditsa, pakuti anakondwera ndi ine.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 18