14. Ndipo anatuma mibvi yace nawabalalitsa;Inde mphezi zaunyinji, nawamwaza.
15. Ndipo zidaoneka zoyendamo madzi,Nafukuka maziko a dziko lapansi,Mwa kudzudzula kwanu, Yehova,Mwa mpumo wa mpweya wa m'mphuno mwanu.
16. Anatuma kucokera m'mwamba, ananditenga;Anandibvuula m'madzi ambiri.
17. Anandipulumutsa ine kwa mdani wanga wamphamvu,Ndi kwa iwo ondida ine, pakuti anandiposa mphamvu.
18. Anandipeza ine tsiku la tsoka langa;Koma Yehova anali mcirikizo wanga.
19. Ananditurutsanso andifikitse motakasuka;Anandilanditsa, pakuti anakondwera ndi ine.