11. Anaika mdima pobisala pace, hema wace womzinga;Mdima wa madzi, makongwa a kuthambo.
12. Mwa kucezemira kunali pamaso pace makongwa anakanganuka,Matalala ndi makala amoto.
13. Ndipo anagunda m'mwamba Yehova,Ndipo Wam'mwambamwamba anamvetsa liu lace;Matalala ndi makala amoto,
14. Ndipo anatuma mibvi yace nawabalalitsa;Inde mphezi zaunyinji, nawamwaza.
15. Ndipo zidaoneka zoyendamo madzi,Nafukuka maziko a dziko lapansi,Mwa kudzudzula kwanu, Yehova,Mwa mpumo wa mpweya wa m'mphuno mwanu.
16. Anatuma kucokera m'mwamba, ananditenga;Anandibvuula m'madzi ambiri.
17. Anandipulumutsa ine kwa mdani wanga wamphamvu,Ndi kwa iwo ondida ine, pakuti anandiposa mphamvu.
18. Anandipeza ine tsiku la tsoka langa;Koma Yehova anali mcirikizo wanga.
19. Ananditurutsanso andifikitse motakasuka;Anandilanditsa, pakuti anakondwera ndi ine.
20. Yehova anandibwezera monga mwa cilungamo canga;Anandisudzula monga mwa kusisira kwa manja anga.
21. Pakuti ndasunga njira za Yehova,Ndipo sindinacitira coipa kusiyana ndi Mulungu wanga.