Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 16:7-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndidzadalitsa Yehova, amene anandicitira uphungu:Usikunso imso zanga zindilangiza.

8. Ndaika Yehova patsogolo panga nthawi zonse:Popeza ali pa dzanja langa lamanja, sindidzagwedezeka.

9. Cifukwa cace wasekera mtima wanga, nukondwera ulemu wanga;Mnofu wanganso udzakhala mokhazikika.

10. Pakuti simudzasiya moyo wanga kumanda;Simudzalola wokondedwa wanu abvunde.

11. Mudzandidziwitsa njira ya moyo:Pankhope panu pali cimwemwe cokwanira;M'dzanja lanu lamanja muli zokondweretsa zomka muyaya.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 16