Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 16:4-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Zidzacuruka zisoni zao za iwo otsata mulungu wina:Sindidzathira nsembe zao zamwazi,Ndipo sindidzachula maina ao pakamwa panga,

5. Yehova ndiye gawo la colowa canga ndi cikho canga:Ndinu wondigwirira colandira canga,

6. Zingwe zandigwera mondikondweretsa;Inde cosiyira cokoma ndiri naco.

7. Ndidzadalitsa Yehova, amene anandicitira uphungu:Usikunso imso zanga zindilangiza.

8. Ndaika Yehova patsogolo panga nthawi zonse:Popeza ali pa dzanja langa lamanja, sindidzagwedezeka.

9. Cifukwa cace wasekera mtima wanga, nukondwera ulemu wanga;Mnofu wanganso udzakhala mokhazikika.

10. Pakuti simudzasiya moyo wanga kumanda;Simudzalola wokondedwa wanu abvunde.

11. Mudzandidziwitsa njira ya moyo:Pankhope panu pali cimwemwe cokwanira;M'dzanja lanu lamanja muli zokondweretsa zomka muyaya.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 16