3. Amene sasinjirira ndi lilime lace,Sacitira mnzace coipa,Ndipo satola msece pa mnansi wace.
4. M'maso mwace munthu woonongeka anyozeka;Koma awacitira ulemu akuopa Yehova.Atalumbira kwa tsoka lace, sasintha ai.
5. Ndarama zace sakongoletsa mofuna phindu lalikuru,Ndipo salandira cokometsera mlandu kutsutsa wosacimwa.Munthu wakucita izi sadzagwedezeka ku nthawi zonse,