Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 149:4-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Popeza Yehova akondwera nao anthu ace;Adzakometsa ofatsa ndi cipulumutso,

5. Okondedwa ace atumphe mokondwera m'ulemu:Apfuule mokondwera pamakama pao,

6. Nyimbo zakukweza Mulungu zikhale pakamwa pao,Ndi lupanga lakuthwa konse konse m'dzanja lao;

7. Kubwezera cilango akunja,Ndi kulanga mitundu ya anthu;

8. Kumanga mafumu ao ndi maunyolo,Ndi omveka ao ndi majerejede acitsulo;

9. Kuwacitira ciweruzo colembedwaco:Ulemu wa okondedwa ace onse ndi uwu.Haleluya.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 149