9. Mapiri ndi zitunda zonse;Mitengo yazipatso ndi yamikungudza yonse:
10. Nyama za kuthengo ndi zoweta zonse;Zokwawa, ndi mbalame zakuuluka;
11. Mafumu a padziko ndi mitundu yonse ya anthu;Zinduna ndi oweruza onse a padziko;
12. Anyamata ndiponso anamwali;Okalamba pamodzi ndi ana:
13. Alemekeze dzina la Yehova;Pakuti dzina lace lokha ndi lokwezeka;Ulemerero wace uli pamwamba pa dziko lapansi ndi thambo.
14. Ndipo anakweza nyanga ya anthu ace,Cilemekezo ca okondedwa ace onse;Ndiwo ana a Israyeli, anthu a pafupi pa Iye,Haleluya,