Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 144:4-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Munthu akunga mpweya;Masiku ace akunga mthunzi wopitirira.

5. Weramutsani thambo lanu, Yehova, nimutsike:Khudzani mapiri ndipo adzafuka.

6. Ng'animitsani mphezi, ndi kuwabalalitsa;Tumizani mibvi yanu, ndi kuwapitikitsa,

7. Turutsani manja anu kucokera m'mwamba;Ndikwatuleni ndi kundilanditsa ku madzi akuru,Ku dzanja la alendo;

8. Amene pakamwa pao alankhula zacabe,Ndi dzanja lao lamanja ndilo dzanja lacinyengo.

9. Ndidzakuyimbirani nyimbo yatsopano, Mulungu;Pa cisakasa ca zingwe khumi ndidzayimbira zakukulemekezani.

10. Ndiye amene apatsa mafumu cipulumutso:Amene alanditsa Davide mtumiki wace ku lupanga loipa.

11. Ndilanditseni ndi kundipulumutsa ku dzanja la alendo,Amene pakamwa pao alankhula zacabe,Ndi dzanja lao lamanja ndilo dzanja lacinyengo.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 144