Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 144:10-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndiye amene apatsa mafumu cipulumutso:Amene alanditsa Davide mtumiki wace ku lupanga loipa.

11. Ndilanditseni ndi kundipulumutsa ku dzanja la alendo,Amene pakamwa pao alankhula zacabe,Ndi dzanja lao lamanja ndilo dzanja lacinyengo.

12. Kuti ana athu amuna akhale ngati mmera udakula usanakhwime;Ana athu akazi ngati nsanamira za kungondya, zosema zikometsere nyumba ya mfumu.

13. Kuti nkhokwe zathu zidzale, kutipatsa za mitundu mitundu;Ndi kuti nkhosa zathu ziswane zikwi zikwi, inde zikwi khumi kubusako.

14. Kuti ng'ombe zathu zikhale zasenza katundu;Ndi kuti pasakhale kupasula linga kapena kuturukamo,Pasakhalenso kupfuula m'makwalala athu.

15. Odala anthu akuona zotere; Odala anthu amene Mulungu wao ndi Yehova.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 144