Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 143:7-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Fulumirani ndiyankheni, Yehova; mzimu wanga ukutha.Musandibisire nkhope yanu;Ndingafanane nao akutsikira kudzenje.

8. Mundimvetse cifundo canu mamawa;Popeza ndikhulupirira Inu:Mundidziwitse njira ndiyendemo;Popeza ndikweza moyo wanga kwa Inu.

9. Mundilanditse kwa adani anga, Yehova;Ndibisala mwa Inu.

10. Mundiphunzitse cokonda Inu; popeza Inu ndinu Mulungu wanga;Mzimu wanu ndi wokoma; munditsogolere kucidikha.

11. Mundipatse moyo, Yehova, cifukwa ca dzina lanu;Mwa cilungamo canu muturutse moyo wanga m'nsautso.

12. Ndipo mwa cifundo canu mundidulire adani anga,Ndipo muononge onse akusautsa moyo wanga;Pakuti ine ndine mtumiki wanu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 143