1. Imvani pemphero langa, Yehova; ndicherere khutu kupemba kwanga;Ndiyankheni mwa cikhulupiriko canu, mwa cilungamo canu.
2. Ndipo musaitane mlandu wa mtumiki wanu;Pakuti pamaso panu sipadzakhala wolungama wamoyo mmodzi yense.
3. Pakuti mdani alondola moyo wanga;Apondereza pansr moyo wanga;Andikhalitsa mumdima monga iwo adafa kale lomwe.
4. Potero mzimu wanga wakomoka mwa ine;Mtima wanga utenga nkhawa m'kati mwanga,
5. Ndikumbukila masiku a kale lomwe;Zija mudazicita ndilingirirapo;Ndikamba pa ndekha za nchito ya manja anu.
6. Nditambalitsira manja anga kwa Inu:Moyo wanga ulira Inu monga dziko lolira mvula.
7. Fulumirani ndiyankheni, Yehova; mzimu wanga ukutha.Musandibisire nkhope yanu;Ndingafanane nao akutsikira kudzenje.
8. Mundimvetse cifundo canu mamawa;Popeza ndikhulupirira Inu:Mundidziwitse njira ndiyendemo;Popeza ndikweza moyo wanga kwa Inu.