Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 140:7-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Yehova Ambuye, ndinu mphamvu ya cipulumutso canga,Munandiphimba mutu wanga tsiku lakulimbana nkhondo.

8. Yehova, musampatse woipa zokhumba iye;Musamthandize zodzipanga zace; angadzikuze.

9. Kunena za mutu wao wa iwo akundizinga,Coipa ca milomo yao ciwaphimbe.

10. Makala amoto awagwere;Aponyedwe kumoto;M'maenje ozama, kuti asaukenso.

11. Munthu wamlomo sadzakhazikika pa dziko lapansi;Coipa cidzamsaka munthu waciwawa kuti cimgwetse.

12. Ndidziwa kuti Yehova adzanenera wozunzika mlandu,Ndi kuweruzira aumphawi,

13. Indedi, olungama adzayamika dzina lanu;Oongoka mtima adzakhala pamaso panu,

Werengani mutu wathunthu Masalmo 140