5. Amene analenga zakumwamba mwanzeru:Pakuti cifundo cace ncosatha.
6. Amene anayala dziko lapansi pamwamba pa madzi:Pakuti cifundo cace ncosatha.
7. Amene analenga miuni yaikuru:Pakuti cifundo cace ncosatha.
8. Dzuwa liweruze usana:Pakuti cifundo cace ncosatha.
9. Mwezi ndi nyenyezi ziweruze usiku;Pakuti cifundo cace ncosatha.
10. Iye amene anapandira Aaigupto ana ao oyamba:Pakuti cifundo cace ncosatha.
11. Naturutsa Israyeli pakati pao;Pakuti cifundo cace ncosatha.
12. Ndi dzanja lamphamvu, ndi mkono wotambasuka:Pakuti cifundo cace ncosatha.
13. Amene anagawa magawo Nyanja Yofiira:Pakuti cifundo cace ncosatha.
14. Napititsa Israyeli pakati pace;Pakuti cifundo cace ncosatha.
15. Nakhutula Farao ndi khamu lace m'Nyanja Yofiira:Pakuti cifundo cace ncosatha.
16. Amene anatsogolera anthu ace m'cipululu:Pakuti cifundo cace ncosatha.
17. Amene anapanda mafumu akulu:Pakuti cifundo cace ncosatha,
18. Ndipo anawapha mafumu omveka:Pakuti cifundo cace ncosatha.