18. Ndipo anawapha mafumu omveka:Pakuti cifundo cace ncosatha.
19. Sihoni mfumu ya Aamori;Pakuti cifundo cace ncosatha.
20. Ndi ogi mfumu ya Basana:Pakuti cifundo cace ncosatha.
21. Ndipo anaperekadzikolaolikhale cosiyira;Pakuti cifundo cace ncosatha.
22. Cosiyira ca kwa Israyeli mtumiki wace;Pakuti cifundo cace ncosatha.
23. Amene anatikumbukila popepuka ife;Pakuti cifundo cace ncosatha.
24. Natikwatula kwa otisautsa;Pakuti cifundo cace ncosatha.
25. Ndiye wakupatsa nyama zonse cakudya;Pakuti cifundo cace ncosatha.
26. Yamikani Mulungu wa kumwamba,Pakuti cifundo cace ncosatha.