Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 132:1-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Yehova, kumbukilani Davide Kuzunzika kwace konse;

2. Kuti analumbira Yehova,Nawindira Wamphamvuyo wa Yakobo, ndi kuti,

3. Ngati ndidzalowa pakhomo pa nyumba yanga,Ngati ndidzakwera pa kama logonapo;

4. Ngati ndidzalola maso anga agone,Kapena zikope zanga ziodzere;

5. Kufikira nditapezera Yehova malo,Cokhalamo Wamphamvuyo wa Yakobo?

6. Taonani, tinacimva m'Efrata;Tinacipeza ku cidikha ca kunkhalango.

7. Tidzalowa mokhalamo Iye;Tidzagwadira ku mpando wa mapazi ace.

8. Ukani, Yehova, lowani ku mpumulo wanu;Inu ndi hema wa mphamvu yanu,

9. Ansembe anu abvale cilungamo;Ndi okondedwa anu apfuule mokondwera.

10. Cifukwa ca Davide mtumiki wanuMusabweze nkhope ya wodzozedwa wanu.

11. Yehova analumbira Davide zoona;Sadzalibweza; ndi kuti,Wa iwo okhala zipatso za thupi lako ndidzaika pa mpando wacifumu wako.

12. Ana ako akasunga cipangano cangaNdi mboni yanga imene ndidzawaphunzitsa,Ana aonso adzakhala pa mpando wanu ku nthawi zonse,

Werengani mutu wathunthu Masalmo 132