Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 128:2-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Pakuti udzadya za nchito ya manja ako;Wodala iwe, ndipo kudzakukomera.

3. Mkazi wako adzanga mpesa wopatsa m'mbali za nyumba yako;Ana ako adzanga timitengo ta azitona pozinga podyera pako.

4. Taonani, m'mwemo adzadalitsikaMunthu wakuopa Yehova.

5. Yehova adzakudalitsa ali m'ZiyoniNdipo udzaona zokoma za Yerusalemu masiku onse a moyo wako.

6. Inde, udzaona zidzukulu zako.Mtendere ukhale ndi Israyeli.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 128