Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 118:9-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Kuthawira kwa Yehova nkokomaKoposa kukhulupirira akulu,

10. Amitundu onse adandizinga,Zedi, m'dzina la Yehova ndidzawaduladula.

11. Adandizinga, inde, adandizinga:Indedi, m'dzinala Yehova ndidzawaduladula.

12. Adandizinga ngati njuci;Anazima ngati moto waminga;Indedi, m'dzina la Yehova ndidzawaduladula.

13. Kundikankha anandikankha ndikadagwa;Koma Yehova anandithandiza.

14. Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;Ndipo anakhala cipulumutso canga.

15. M'mahema a olungama muli liu lakupfuula mokondwera ndi la cipulumutso:

16. Dzanja lamanja la Yehova licita mwamphamvu.

17. Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo,Ndipo ndidzafotokozera nchito za Yehova.

18. Kulanga anandilangadi Yehova:Koma sanandipereka kuimfa ai.

19. Nditsegulireni zipata za cilungamo;Ndidzalowamo, ndidzayamika Yehova.

20. Cipata ca Yehova ndi ici;Olungama adzalowamo.

21. Ndidzakuyamikani, popeza munandiyankha,Ndipo munakhala cipulumutso canga,

Werengani mutu wathunthu Masalmo 118