Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 118:21-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndidzakuyamikani, popeza munandiyankha,Ndipo munakhala cipulumutso canga,

22. Mwala umene omangawo anaukanaWakhala mutu wa pangondya.

23. Ici cidzera kwa Yehova;Ncodabwiza ici pamaso pathu.

24. Tsiku ili ndilo adaliika Yehova;Tidzasekera ndi kukondwera m'mwemo.

25. Tikupemphani, Yehova, tipulumutseni tsopano;Tikupemphani, Yehova, tipindulitseni tsopano.

26. Wodala wakudzayo m'dzina la Yehova;Takudalitsani kocokera m'nyumba ya Yehova.

27. Yehova ndiye Mulungu, amene anatiunikira;Mangani nsembe ndi zingwe, ku nyanga za guwa la nsembe.

28. Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani;Ndinu Mulungu wanga, ndidzakukwezani.

29. Yamikani Yehova, pakuti Iye ndiye wabwino,Pakuti cifundo cace ncosatha.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 118