Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 109:7-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ponenedwa mlandu wace aturuke wotsutsika;Ndi pemphero lace likhale ngati kucimwa.

8. Masiku ace akhale owerengeka;Wina alandire udindo wace.

9. Ana ace akhale amasiye, Ndi mkazi wace wamasiye.

10. Ana ace akhale amcirakuyenda ndi opemphapempha;Afunefune zosowa zao kucokera m'mabwinja mwao.

11. Wokongoletsa agwire zonse ali nazo;Ndi alendo alande za nchito yace.

12. Pasakhale munthu wakumdtira cifundo;Kapena kucitira cokoma ana ace amasiye.

13. Zidzukulu zace zidulidwe;Dzina lao lifafanizidwe mu mbadwo ukudza.

14. Mphulupulu za makolo ace zikumbukike ndi Yehova;Ndi cimo la mai wace lisafafanizidwe.

15. Zikhale pamaso pa Yehova cikhalire,Kuti adule cikumbukilo cao kucicotsera ku dziko lapansi.

16. Cifukwa kuti sanakumbukila kucita cifundo,Koma analondola wozunzika ndi waumphawi,Ndi wosweka mtima, kuti awaphe.

17. Inde, anakonda kutemberera, ndipo kudamdzera mwini;Sanakondwera nako kudalitsa, ndipo kudamkhalira kutali.

18. Anabvalanso temberero ngati maraya,Ndipo lidamlowa m'kati mwace ngati madzi,Ndi ngati mafuta m'mafupa ace.

19. Limkhalire ngati cobvala adzikuta naco,Ndi lamba limene adzimangirira nalo m'cuuno cimangirire,

20. Ici cikhale mphotho ya otsutsana nane yowapatsa Yehova,Ndi ya iwo akunenera coipa moyo wanga.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 109