Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 109:6-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Muike munthu woipa akhale mkuru wace;Ndi mdani aime pa dzanja lamanja lace.

7. Ponenedwa mlandu wace aturuke wotsutsika;Ndi pemphero lace likhale ngati kucimwa.

8. Masiku ace akhale owerengeka;Wina alandire udindo wace.

9. Ana ace akhale amasiye, Ndi mkazi wace wamasiye.

10. Ana ace akhale amcirakuyenda ndi opemphapempha;Afunefune zosowa zao kucokera m'mabwinja mwao.

11. Wokongoletsa agwire zonse ali nazo;Ndi alendo alande za nchito yace.

12. Pasakhale munthu wakumdtira cifundo;Kapena kucitira cokoma ana ace amasiye.

13. Zidzukulu zace zidulidwe;Dzina lao lifafanizidwe mu mbadwo ukudza.

14. Mphulupulu za makolo ace zikumbukike ndi Yehova;Ndi cimo la mai wace lisafafanizidwe.

15. Zikhale pamaso pa Yehova cikhalire,Kuti adule cikumbukilo cao kucicotsera ku dziko lapansi.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 109