Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 109:19-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Limkhalire ngati cobvala adzikuta naco,Ndi lamba limene adzimangirira nalo m'cuuno cimangirire,

20. Ici cikhale mphotho ya otsutsana nane yowapatsa Yehova,Ndi ya iwo akunenera coipa moyo wanga.

21. Koma Inu, Yehova Ambuye, mucite nane cifukwa ca dzina lanu;Ndilanditseni popeza cifundo canu ndi cabwino.

22. Pakuti ine ndine wozunzika ndi waumphawi,Ndi mtima wanga walaswa m'kati mwanga.

23. Ndamuka ngati mthunzi womka m'taliNdiingidwa kwina ndi kwina ngati dzombe.

24. Mabondo anga agwedezeka cifukwa ca kusala;Ndi mnofu wanga waonda posowa mafuta.

25. Ndiwakhaliranso cotonza;Pakundiona apukusa mutu.

26. Ndithandizeni Yehova, Mulungu wanga:Ndipulumutseni monga mwa cifundo canu;

27. Kuti adziwe kuti ici ndi dzanja lanu;Kuti Inu Yehova munacicita.

28. Atemberere iwowa, koma mudalitse ndinu;Pakuuka iwowa adzacita manyazi, koma mtumiki wanu adzakondwera.

29. Otsutsana nane abvale manyazi,Nadzikute naco cisokonezo cao ngati ndi copfunda.

30. Ndidzayamika Yehova kwakukuru pakamwa panga;Ndi pakati pa anthu aunyinji ndidzamlemekeza.

31. Popeza adzaima pa dzanja lamanja la waumphawiKumpulumutsa kwa iwo akuweruza koipa moyo wace.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 109